Gawo #310, June 28, 2022

Atsogoleri Muutumiki Amafunsa Omwe Akutsatila: "Kodi Musiye Kupanga Chani?"

Atsogoleri onse amapatsako ntchito ena muzolinga zawo zokwanilitsa masomphenya, kuwonjezela pa ntchito "zoti azazichite" zomwe zili mundandanda wawo. Koma atsogoleri muutumiki amaimitsa kupeleka ntchito kwa ena kwa nthawi yabwino kuti afunse funso losiyana la otsatila awo: "Kodi musiye kupanga chani?" Amaphunzila kuchoka kwa Yetelo, apongozi amuna a Mose.

Eksodo 18

13 Mmawa mwake, Mose anakhala pa mpando kuti aweruze milandu ya anthu. Anthu anayima momuzungulira kuyambira mmawa mpaka madzulo.

14 Mpongozi wa Mose ataona zonse zimene iye amawachitira anthu anati, “Nʼchiyani chimene mukuwachitira anthuwa? Nʼchifukwa chiyani mulipo nokha woweruza, pamene anthu onsewa ayimirira kuyambira mmawa mpaka madzulo?”, (werengani ndime ya 13-27, mmunsimu,kuti mumalizitse ndimeyi) Yetelo mokhuzidwa amamufunsa Mose kuti aganize za zomwe amachita zimene amafunika kuti azisiye. Mose amachita chinthu chachikulu ndi chabwino; amatumikila dziko! Anali otanganidwa kuchoka" mmawa mpaka madzulo" kuchita zomwe amaganiza kuti ndi ntchito yake. Aliyense omuzungulila amamusilira kwambiri ndi ulemu waukulu monga mtsogoleri wamphamvu. Koma Yetelo akubwela patsogolo ndikumufunsa mafunso olimba omwe mwachangu anaumba Mose muulendo wake wautsogoleri. Atsogoleri muutumiki amapanga chimodzimodzi kwa omwe akuwatsogolera.

Atsogoleri Muutumiki amafunsa kodi musiye kupanga chani? Popewa kulema .

Yetero akumufotokozela Mose kuti ngati atasiya kuchita zinthuzina zomwe amachita, akanakwanitsa "kuthana ndi kulema" (Exodo 18:23). Mose amagwila ntchito mozipereka Koma sakanakwanitsa kupanga izi kwanthawi yaitali ya utsogoleri wake. Yetero anali okhuzidwa kuti Mose sakadatha kupitiliza mulingo wantchito yomwe amagwila. Atsogoleri muutumiki amafuna zabwino kwa omwe amawatsogolera. Amawona omwe akuwatsatila osati ngati makina owabweletsela phindu mopitilila Koma ngati anthu omwe ali ndi mphatso koma ali ndi malile pokhala kuti Iwo ndianthu! Atsogoleri muutumiki osakakamiza anthu mopyolera kuthekela kwa mthupi mwawo ndi thanzi lawo. Mmalomwake, amaphunzila kufunsanso amene akuwatsogolera, "kodi musiye kupanga chani kuti mupewe kulema?”

Atsogoleri muutumiki amafunsa amafunsa "kodi musiye kupanga chani?" Kuti ayike chindunji chawo pa zomwe amatha kuchita bwino.

Yetero akumupatsa uphungu Mose kuti akagawa chimtolo, iye ayika chindunji chake pa milandu ikulu ikulu yomwe ndiyovuta. Akwanitsa kugwilitsa ntchito mphamvu zake munjila yabwino potumikila dziko. Atsogoleri omwe amakhala otanganidwa kuchoka mmawa mpaka madzulo nthawi zambili sakwanitsa kutumikila mudela lomwe Iwo amachita bwino. Mmalomwake, akupanga tizinthu tochepa nsinkhu koma tambili ndi tabwino pa ndandanda wawo wa "zoti achite" koma osakhala ndi chindunji pa zinthu zikuluzikulu zofunika zomwe palibe winanso angazichite koma iwowo. Atsogoleri muutumiki amabweleza funsoba Yetero kwa Iwo akuwatsogolera kuwathandiza kuganiza mwakuya za magawo omwe Iwo amatha kuchita bwino. Amafunsa, "kodi musiye kupanga chani zomwe simumatha kuzichita bwino?" Funso lawo limatakasa kuganiza mwinanso kusintha kumene pa zomwe zili ntchito zoti azigwila zomwe zimamasula munthu kutumikila mumadela omwe amachita bwino kwambili.

Atsogoleri muutumiki amafunsa "kodi musiye kupanga chani?" Kuti aphunzitse ena

Yetero anafunsa Mose chifukwa chomwe amagwilira yekha ntchito "pomwe ena onse analipo kumangomuyang'anira". Anazindikila kuti ngati Mose amagwira ntchito yonse yekha, enawo sakanaphunzitsika. Anali ndi mphatso ndi kuthekela zomwe sizimagwilitsidwa ntchito. Yetero akumupempha Mose kuti ntchito zina apereke kwa ena kuti enawo akule! Atsogoleri muutumiki samangoyan'gana zinthu zomwe akuyenela kusiya kuzichita, koma amatembenukila kwa omwe amatsatila ndikuwafunsa Kodi wina ndani angachite zomwe mukuchita panozi? Kodi muzasiya liti kuzichita kuti ena akule?

Amafunsa mmalo mongowauza chifukwa amafuna munthu akumutsogolerayo kuganiza pa iye yekha ndi kukula mikuthekela komwe alinako Iwo eni kotsogolera. Akhozanso kufunsa chifukwa, kusiyana ndi Yetero, sakuziwa zinthu pa ndandanda wawo wa zoti achite zomwe akulemedwa ndi kupanikizika nazo.

Zoti tilingalire ndikukambirana:

  • Sankhani mmodzi mwa anthu omwe akwanitsa kupanga zithu pa gulu lanu mumuganizile. Munthu ameneyo ndi ndani? Sankhani mafunso olingana kuchoka pa ndandanda wammunsiwu pokonzekela nthawi yanu ndi munthu ameneyu. Kenaka kumanani nawo ndikuwatumikila pofunsa zomwe muli nazo pa ndandanda wanuwo.
  • Kodi mukupanga zinthu ziti zomwe zimakulemetsani?
  • Kodi mukuyenela kusiya kupanga ziti ndi cholinga choti thanzi lanu ndi moyo wanu usakhale pa chiophyezo?
  • Kodi mulingo wamachitidwe anu azinthu panopa, zomwe mukuchitazo zikhala zikupitililabe mpaka kale? Ngati sichoncho, Kodi ndi zinthu ziti zomwe mukuyenela kusiya kupanga?
  • Pa zonse mukuchitila bungwe limeneli, Kodi mumachita chani chomwe chimaonetsa kuti ndi mbali yanu yomwe mumachita bwino?
  • Pa ntchito zomwe mumagwila kawilikawili, ndi ziti zomwe sizili mmadela anu ochitabwino? Kodi mungasiye bwanji kuzichita?
  • Ndiziti pa ntchito zomwe mukugwira pano zomwe wena akhoza kugwira? Kodi chikufinika ndi chani kwa inu kuti mupeleke ntchito imeneyi kwa anthuwa?
  • Kodi chimachitika ndichani kwa omwe ali pansi panu paomwe mupitiliza kugwila ntchito yomweyomweyo kwa nthawi yaitali? Kodi mukupeleka danga loti kuthekela kwawo kuzindikilike?

Mpaka nthawi ina, ine wanu wapaulendo,

Jon Byler

 

Muphunziro lotsatilali, tiona funso lina lomwe atsogoleri otumikila amadzifunsa okha: Kodi ndiyambe kuchita chani?

Nayi nkhani yonse ya Yetero akumulangiza Mose.

Eksodo 18

13 Mmawa mwake, Mose anakhala pa mpando kuti aweruze milandu ya anthu. Anthu anayima momuzungulira kuyambira mmawa mpaka madzulo.

14 Mpongozi wa Mose ataona zonse zimene iye amawachitira anthu anati, “Nʼchiyani chimene mukuwachitira anthuwa? Nʼchifukwa chiyani mulipo nokha woweruza, pamene anthu onsewa ayimirira kuyambira mmawa mpaka madzulo?”

15 Mose anamuyankha kuti, “Chifukwa anthuwa anabwera kwa ine kudzafunsa zimene Mulungu akufuna.

16 Ngati munthu akangana ndi mʼbale wake, onse awiri amabwera kwa ine, ndipo ine ndimawaweruza. Ndimawawuzanso malamulo a Mulungu ndi malangizo ake.”

17 Mpongozi wa Mose anayankha kuti, “Zimene mukuchitazi si zabwino.

18 Ntchitoyi ndi yayikulu kuposa mphamvu zanu. Inu simungathe kuyigwira nokha. Inu pamodzi ndi anthuwa amene amabwera kwa inu mudzatopa.

19 Tsono tamverani ndikulangizeni, ndipo Mulungu akhale nanu. Inu muziwayimirira anthuwa pamaso pa Mulungu, ndipo mikangano yawo muzibwera nayo kwa Iye.

20 Aphunzitseni mawu ndi malangizo a Mulungu. Aphunzitseni mmene ayenera kukhalira ndi zimene ayenera kuchita.

21 Koma sankhani amuna odziwa ntchito yawo, anthu owopa Mulungu, anthu odalirika amene amadana ndi kupeza phindu mwachinyengo. Tsono muwayike kuti akhale oyangʼanira anthu motere: atsogoleri a anthu 1,000, ena a anthu 100, ena a anthu 50 ndi ena a anthu khumi.

22 Tsono amenewa aziweruza anthu nthawi zonse. Mlandu uliwonse waukulu azibwera nawo kwa inu, koma mlandu waungʼono aziweruza okha. Izi zidzachititsa kuti ntchito yanu ipepuke, popeza mudzagwira ntchito mothandizana.

23 Ngati mutsatira malangizowa monga mmene Mulungu wakulamulirani ndiye kuti simudzafowoka ndipo anthu onsewa adzapita kwawo mu mtendere.”

24 Mose anamvera mpongozi wake ndi kuchita zonse zimene iye ananena.

25 Iye anasankha amuna odziwa bwino ntchito zawo ndipo anawayika kuti akhale atsogoleri, oyangʼanira anthu motere: atsogoleri a anthu 1,000, ena a anthu 500, ena a anthu makumi asanu ndi ena a anthu khumi.

26 Iwowa ankaweruza anthu nthawi zonse. Milandu yovuta ankabwera nayo kwa Mose, koma yosavuta ankayiweruza okha.

27 Kenaka Mose analola kuti mpongozi wake, Yetero anyamuke kubwerera ku dziko la kwawo.

Tumizani kwa anzanu omwe akufuna kutsatila
chitsanzo cha Yesu potsogolera ngati otumikira.Angathe kulembetsa mwaulere komanso kuona magawo akale.mukafuna kupeza magawo akale , dinani apa.Magawo awa amatanthauziridwa mchichewa ndi abusa Grace Kacheto Saizi, gracekacheto@yahoo.com

Reflections for Serving Leaders is published by Center for Serving Leadership and Jon Byler. Copyright, 2023

Unsubscribe   |   Modify your subscription   |   View online