Gawo #300, November 9, 2022

Boazi:Kutumikira Pokangitsa Zinthu Kutheka

Taona kale kuti Boazi anali munthu wa chikhalidwe chabwino. Mtima wake ofuna kutumikira unkatsogolera machitidwe ake pomwe amakhala mwabwino ndi anthu, kulemekeza ofooka , kupereka molowa manja ndi kusunga mau ake. Mu phunziro lotsirizali tiona momwe  Boazi anatumikilira popanga zinthu kutheka.

Rute 4

1 Nthawi yomweyo Bowazi anapita ku chipata cha mzinda ndi kukhala pansi kumeneko pabwalo losonkhanira. Tsono anangoona wachibale woyenera kulowa chokolo uja akufika. Ndipo Bowazi anati, “Patukirani kuno, bwenzi langa. Mubwere mudzakhale apa.” Choncho anapatuka nakakhala pansi.

2 Bowazi anayitananso akuluakulu khumi a mu mzindamo nati, “Dzakhaleni pansi apa,” ndipo anadzakhala pansi.

3 Kenaka anamuwuza oyenera kulowa chokolo uja kuti, “Naomi amene wabwera kuchoka ku Mowabu akugulitsa malo amene anali a malemu Elimeleki, mʼbale wathu uja.

Atsogoleri onse ndi anthu ochitapo kanthu;amapanga zinthu kutheka.Boazi akuonetsera momwe atsogoleri mu utumiki amapangitsira zithu kutheka munjira zomwe omaika chidwi chawo pa ena.

Atsogoleri mu Utumiki amapangitsa zinthu kutheka pogwiritsa ntchito nzeru ina.

Rute atabwera kuchokera kwa Boazi usiku, apongozi ake anamuuza.

Rute 3

18 Kenaka Naomi anati, “Mwana wanga, dikira mpaka titaona mmene zinthu zikhalire chifukwa munthuyu salekera pomwepo, mpaka zinthuzi zitakonzeka lero.”

Monga momwe Naomi anayembekezera Boazi anapanga zomwezo pompo pompo.Boazi anapita pa bwalo la mmudzi komwe zinthu zimachitikira.Anafika pa nthawi yoyenera ndipo anali okonzeka kuchita nthawi yomweyo atangofika. Anaitanitsa mkumano ndi kupereka mutu wake wa msonkhanowo momveka bwino. Boazi amachita zomwe atsogoleri amachita mwabwino,kupeza nzeru ina kuti zinthu zitheke.Koma chifukwa chani amachita izi?

Amayankha pa pempho la Rute ,mzimayi wamasiye. Monga wachibale anali ndi udindo pa chikhalidwe chawo kuthandiza Rute yemwe anali ndi chosowa. Ngakhale mwachiziwikile amapezapo mkazi kuchokera pa nzeru imeneyi koma machitidwe ake sadali ozikonda. Atsogoleri mu utumiki amapereka nzeru kuti apangitse zinthu kutheka koma amachita izi kuchokera mu mtima omwe umaika chidwi pa ena kopsosa pa Iwo eni.

Atsogoleri mu utumiki amapangitsa zinthu kutheka popanga ukadziotche.

Kulowa chokolo kunaali kupanga ukadziotche. Wachibale amayembekezeka kutenga chuma cha munthu amene wamwalira, komanso kukwatira mkazi osiyidwayo. Ana obadwa kuchokera kwa ubale umenewu amayenera kukhala a malemu mamuna wa mkaziyo  zomwe zimagawa munda wa olowa chokoloyo.Boazi anaipereka nkhaniyo kwa m'bale wake podziwa kuti bambo ameneyu ndi yemwe amayenera kulowa chokolo kwa Naomi.Akadavomera, Rute  ndi chuma zikanapita kwa iye mmalo mwa Boazi. Boazi anali ofuna kupanga ukadziotche pomwe wachibaleyu samafuna. Komanso,anali ofuna kuchita zomwe atsogoleri amachita, kupanga ukadziotche kuti zinthu ziyende.Koma atsogoleri mu utumiki, ngati Boazi, amapanga ukadziotche osati ongopindulira iwo okha komanso Iwo amene amawatumikira.

Atsogoleri mu utumiki amapangitsa zinthu kutheka petenga udindo

Pamene wachibale uja anakana ,Boazi anali okonzeka kutenga udindo.

Rute 4

9 Ndipo Bowazi anawuza akuluakuluwo ndi anthu onse aja kuti, “Nonsenu ndinu mboni lero, kuti ine ndagula kwa Naomi zonse zimene zinali za malemu Elimeleki, zonse zimene zinali za malemu Kiliyoni ndiponso za malemu Maloni.

10 Ndatenganso Rute Mmowabu uja mkazi wa malemu Maloni, kuti akhale mkazi wanga, kuti dzina la malemu Maloni lisungike pa cholowa chake, ndipo lisafafanizike pakati pa abale ake ngakhalenso mʼmudzi mwake. Nonsenu ndinu mboni lero lino.”

atsogoleri onse amapanga zinthu kutheka potenga udindo.Boazi, ngati mtsogoleri, anatenga mbali yomwe chidwi chinali pa ena, osati pa iye yekha. Atsogoleri otumikita lowanipo ndikutenga udindo omwe upindilire ena.

Moyo wa Boazi ndi chitsanzo kwa atsogoleri onse muutumiki. Anali munthu "omvetsetsa" yemwe machitidwe ake a utsogoleri ankasefukira kuchoka mumtima mwake kuti atumikire. Tsatani chitsanzo chake ndi omwe mukuwatumikira lero!

Zoti tilingalire ndi kukambirana

  • Werenganinso machaputala anayi a buku la Rute kuyang'ana zisonyezo zina za mmene Boazi anapangira zinthu kutheka .Kodi mukuonapo chani?Kodi ndimunjira iti mukuphunzira kuchokera pa chitsanzo chake?
  • Kodi chimodzi mwa njira yomaliza yofunikira yomwe ndinagwiritsa ntchito popangitsa zinthu kutheka ndi iti?Kodi cholinga choyambilira ndinaika chidwi pa ine mwini kapena pa ena?Kodi ichi chikulankhula chani za mtima wanga mmene uliri ndipo ichi chikukhudza bwanji utsogoleri wanga?
  • Kodi ndi munjira iti yomwe ndingapange ukadziotche omwe umapindulira ena mu udindo wanga panopa?Kodi ndili ndi cholinga chopereka dipo lochuluka kapena lochepetsetsa?Kodi zimenezi zikhudza bwanji utsogoleri wanga?
  • Kodi pali dera la utsogoleri wanga limene ndasiya kutenga udindo,kapena powopa zomwe ndingapereke?Kodi chitsanzo cha Boazi chikundiitanira Ku kupita patsogolo?

 

Mpaka nthawi ina, ine wanu wapaulendo,

Jon Byler

 

Mu nkhami yotsatirayi ,tiona mozama mmene Boazi anatumikilira  posunga mau make.

Tumizani kwa anzanu omwe akufuna kutsatila
chitsanzo cha Yesu potsogolera ngati otumikira.Angathe kulembetsa mwaulere komanso kuona magawo akale.mukafuna kupeza magawo akale , dinani apa.Magawo awa amatanthauziridwa mchichewa ndi abusa Grace Kacheto Saizi, gracekacheto@yahoo.com

Reflections for Serving Leaders is published by Center for Serving Leadership and Jon Byler. Copyright, 2022

Unsubscribe   |   Modify your subscription   |   View online