Gawo #298, October 12, 2022

Boazi:Kutumikira pa Kupeleka Moolowamanja

Tawona kale kuti Boazi anali "munthu wamaimidwe abwino". Khalidwe lake linaumba machitidwe ake a utsogoleri munjira yomwe amakhalira bwino ndi anthu ndi mmene amachitira ndi ofooka. Kupereka kwake moolowa manja kunaonetseranso khalidwe lake. Kawiri munkhaniyi Boazi anapereka moolowa manja kwa Rute.

Rute 2

14 Nthawi ya chakudya cha masana Bowazi anati kwa iye, “Bwera kuno, utenge buledi ndi kusunsa nthongo mu vinyo.” Choncho anakhala pansi pafupi ndi okololawo, ndipo Bowazi anamupatsa chakudya ndi nyama yowotcha. Anadya chilichonse amafuna ndipo chakudya china chinatsalako.

Rute 3

15 Bowazi anati kwa Rute, “Bwera mnacho kuno chofunda wavalacho ndipo uchiyale pansi.” Ndipo atayala, Bowazi anathira makilogalamu makumi awiri a barele ndi kumusenzetsa Rute. Rute anapita nakalowa mu mzinda.

Boazi anagawana chakudya chake ndi Rute mmunda kenaka anampatsanso chopereka moolowa manja cha chimanga.,chambiri chomwe iye akanakwanitsa kunyamula! Ndipo Rute sanali yekhayo yemwe anapindula kuchoka Ku mtima wake opereka moolowa manja. Panalinso ena omwe anadya limodzi mokondwa ndi Boazi ndi azimayi enanso omwe amagwira ntchito mmundamo. Boazi amatha Kupereka moolowa manja chifukwa mtima wake unali pa kutumikira. Kupereka kwake ndi chitsanzo kwa atsogoleri onse otumikira.

*Atsogoleri mu utumiki amapereka moolowa mania pomwe akuika chidwi chawo pa ena osati pa Iwo okha.*

Pomwe Boazi anakhala pansi kuti adye chakudya chake, akanangothokoza Mulungu chifukwa chompatsa chakudyacho. Koma anayang'ana yang'ana ndikuona kuti Rute analibe choti adye.Kotero ,anagawana naye, kupereka chake chabwino, osati zotsalira. Chidwi chake sichinali pa zozowa zake, koma pa zosowa za ena.Atsogoleri ambiri amazikundikira okha pamene akutsogolera.Amaganizira za zolinga zawo zoti afikire, za ndondomeko zawo ndipo amaona ena  ngati njira yowathandizila kukwaniritsa mathero awo. Koma atsogoleri mu mutumiki  amaona udindo wawo ngati mwayi otumikira omwe akuwatsogolera.Amaika chidwi chawo pa ena  Iwo asanaziikemo.Chidwi chawo ndi cha kunja osati cha mkati mwawo.

*Atsogoleri mu utumiki amapereka mokondwela  pomwe akuika chidwi chawo pa kupereka osati pa kulandila.*

Boazi anatsegula munda ndipo chilungamo chake amayembekezela zokolola.Koma chidwi chake chinali pa kupereka mmalo mopeza.Anawona chimanga ngati chinthu chomwe sichikanakwanilitsa zosowa zake zokha koma chomulora kupereka kwa ena  ngati Rute.Iye anadziwa kuti opereka amalandilanso,koma cholinga chake chinali pongopereka ndi mtima okondwera.Atsogoleri ambiri ali pa maudindo a atsogoleri pa cholinga chopeza kuchokera muutsogoleri.Izi ndi monga mphatso za ndalama,zolipira milandu,kukhala ndi ulamuliro kapena kukonda mphanvu za ulamuliro.Koma atsogoleri mu utumiki amatsogolera kuti  akapereke.Samaika mulingo wa kupambana kwawo pa zomwe amapeza koma pa zomwe amapereka.Chidwi chawo chili pa kupereka osati pa kupeza.

*Atsogoleri mu utumiki amapereka moolowa manja pomwe akuika chidwi chawo pa kuchuluka osati pa kusowa kwa zinthu.*

Boazi sanayang'ane pa zokolora zake ndi kuganiza kuti kupereka kumubweretsela  kuluza pa zokolora zake.Sanaganizire kuti kugawa chakudwa chake kumupangitsa kukhala ndi njala.Anali ndi lingaliro la kuchuluka .Anazindikira kuti chinalipo cha onse ndipo kuti kupereka kumabweretsa dalitso mmalo mwa kusowa.Sadadziwe munthawiyi kuti azapeza mkazi ndi malo mu mbiri ya Israel ya kupereka kwake.Koma Boazi anali ataphunzila kale kuti atsogoleri omwe amapereka ndi omwenso amapeza phindu.Atsogoleri ambiri amaona chithu chovuta kupereka chifukwa amaona kuti zinthuzo ndi zopezeka patalipatali.Amaganiza kuti ngati apereka ,sangapeze zokwanila iwowo.Atsogoleri amenewa amapereka pokhapokha ngati awona kuti ali ndi zochuluka.Atsogoleri oganiza moterewa sapezanso zambiri kuti apereke!Koma atsogoleri mu utumiki amaona dziko la zochu

luka.Amapeza madalitso mu kupereka ndi kupeza chimwemwe cha kulandiranso. Kupereka kwawo kumatakasa ena kuti aperekenso, ndipo dziko limayamba kuyenda munjira zokongola. Chidwi chawo chili pa zochuluka, osati pa  kupelewera.

Zoti tilingalire ndi kukambirana

  • Werenganinso ma chaputala 4 a Rute poyang'ana zina zowonetsa mmene Boazi amaperekera moolowa manja.Mukuonapo chani? Munjira yanji omwe mungaphunzilirepo pa chitsanzo chake?
  • Ndili mu utsogoleri chifukwa cha zomwe ndikufuna kupeza kapena chifukwa cha zomwe ndikufuna kupereka? Munjira yanji yomwe zochita zanga mu sabata yapitayi zaonetsera machitidwe a mtima umenewu?
  • Pamene ndikuika mulingo wa kupambana kodi ndimayang'ana pa zomwe ndikupeza mu utsogoleri wanga kapena pa zomwe ndimatha kupereka? Kodi ndi njira iti yomwe ndingatsate kuti ndizipereka moolowa manja? kodi ndi zithu ziti zomwe ndingapereke kupatula zooneka ndi maso?
  • Kodi chidwi changa poyamba chili pa kuchuluka kapena kuperewela? kodi Izi zikhudza bwanji kupereka kwanga moolowa manja ndi mokondwera?Ndichite chani kuti ndichulukitse chidwi changa pa kuchuluka?
  • Kodi ndili ndi chani chomwe ndingapereke? (ganizilani chogwirika chomwe mungapereke kwa wina wake.Ichi chitha kukhala chithu chomwe ulinacho ,mphatso ya nthawi,ndalama zosonkha kwa yemwe ali ndi chosowa,ndi zina zotero.Pezani China chake chomwe mungachite kuti mupereke.Kenaka lingalirani pa zomwe zikuchitika mu mtima mwanu)

 

Mpaka nthawi ina, one wanu wa paulendo,

Jon Byler

 

Mu nkhami yotsatirayi ,tiona mozama mmene Boazi anatumikilira  posunga mau make.

Tumizani kwa anzanu omwe akufuna kutsatila
chitsanzo cha Yesu potsogolera ngati otumikira.Angathe kulembetsa mwaulere komanso kuona magawo akale.mukafuna kupeza magawo akale , dinani apa.Magawo awa amatanthauziridwa mchichewa ndi abusa Grace Kacheto Saizi, gracekacheto@yahoo.com

Reflections for Serving Leaders is published by Center for Serving Leadership and Jon Byler. Copyright, 2022

Unsubscribe   |   Modify your subscription   |   View online