Gawo #289, May 11, 2022

Yesu: Thamangirani Ku Cholinga Chachikulu

Yesu anaphunzitsa ndikuwonetsela  utsogoleri omwe unali osiyana mu nthawi yake ndipo omwe ukupitiliza kubetchela ndi kusintha miyanda miyanda ya atsogoleri kwa zaka zokwana 2000 zotsatila.Utsogoleri wa Yesu ndi chitsanzo chathu cha utsogoleri otumikira.Mu mutu uwu tiwona mmene Yesu anawonetsera  zithu zisanu mwadala pomwe ankatuma ophunzira ake 72 mu Luka 10:1-24.Atsogoleri muutumiki  phunzirani kwa iye ndipo tsatirani njira zisanuzi zomwe zimapanga maziko a Chitsanzo Cha Mtsogoleri Otumikira.Choyamba chomwe Yesu anawonetsera  ndi Kuthamangira Ku Cholinga Chachikulu.

1 Zitatha izi Ambuye anasankha enanso 72   ndikuwatumiza iwo awiri awiri Ku mzinda uliwonse umene iye amafuna kupitako.

2 Anati kwa iwo,"Zokolora ndi zambiri,koma antchito ndi opelewera.Pemphani Ambuye wa Zokolora ,kotero,kuti atumize antchito Ku munda wake wakholora.(Luka 10:1-24).

Yesu amafuna kutumiza ogwira ntchito 72 ndipo anali ndi cholinga chowonekeratu.Koma asanawatume ,anafotokozeratu monveka bwino  masomphenya  kapena

Chomwe tikutcha cholinga chachikulu.Atsogoleri Otumikira phunzirani mphamvu ya cholinga chachikulu kuchokera pa chitsanzo chake.

Cholinga chachikulu  chimawonetsera chitsogozo.

Yesu anawauza ophunzira ake kuti apite mmadera ndi mmalo omwe iye amafuna awayendele.Mau ake anapereka chitsogozo kwa iwo.Sadangoziwa komwe amafuna kuti apite;komanso adadziwa komwe samayenera kupita!Cholinga chachikulu chimaonetsera chitsogozo. Atsogoleri ena amauza wanthu kuti apange ntchito  koma samawalumikiza ku ntchito za Ku cholinga chachikulu.

Atsogoleri Otumikira fotokozerani cholinga chachikulu kuti chithandize otsatira Ku chindunji cha komwe akupita.Amaunika zochitika zonse powona mmene akutengera bungwe Ku cholinga  chachikulu.

Cholinga chachikulu chimatsimikizira tanthauzo

Yesu anapempha ophunzira ake kuti atsogole Ku maderawa.Koma kupita kwawo kunali "kokonzekera kholora" lomwe limabwera.Yesu mosamala anawadziwitsa Iwo kuti  zomwe amachita zinali zokonzekera 

chinachake chachikulu ndichofunika kwambiri.Anapereka tanthauzo la ntchito  yawo.Atsogoleri ambiri amangowona ngati otsatira amangofuna ka mnunsu kapena  mutu wa chinthu kuti azigwira ntchito. Koma Yesu akukumbutsa   atsogoleri onse  mu utumiki  anthu amafuna adziwe  kuti ntchito yawo ili ndi tanthauzo komanso cholinga chopambana  mwaiwo wokha.Atsogoleri muutumiki amathandiza wanthu kuti awone mmene machitidwe awo angatsogolere ku kukwaniritsa cholinga chachikulu.

Cholinga chachikulu chimathandizira kuzipereka

Yesu sadangotsegula maso awo ku cholinga chomvekabwino cha ntchito amawauza kuti ayigwireyo,komanso anawaitanira ku kuganiza kopapyola ntchitoyo kwa tsiku limenero.Anawaitanira ku kupemphelera antchito ambiri!Cholinga chachikulu chimatakasa  kuzipereka kuchokera kwa ena.Pomwe akuvomereza masomphenya ngati awo,amayamba kutenga cholinga kukhala chawo ndikuitana ena kupanga nawo zomwe akuchita.Amathandiza nawo mtsogoleri ngati eni masomphenya. Pa ichi amakhala ozipereka kwatunthu ku cholinga chachikulu ndipo amakhala ofuna kuchita zonse zofunika kuti zichitike kuti zikwaniritse  ntchito.

Atsogoleri muutumiki amatsogolera bwino pomwe akutsatira chitsanzo cha Yesu.amafotokoza momveka bwino cholinga chachikulu cha bungwe lawo ndi kusunga mwapamwamba masomphenyawa nthawi zonse kwa anthu omwe akuwatumikira.Amamangikira ntchito iliyonse ndi kuzipereka kwawo ku cholinga chachikulu ndipo pakupanga izi amapereka tanthauzo ndi cholinga kwa aliyense.Amagwira ntchito molimbika  kuti awonetsetse munthu aliyense mu bungwemo,kuyambira wapamwamba mpaka wapansi ,amvetsetse kuti ali nawo mugulu lomwe likubweretsa kusintha.Limeneli ndiye gulu lomwe tonse tikufuna tikhalemo ndipo ndi moteromo momwe Yesu anatsogolera gulu lake!

Zina zomwe tingalingalirepo ndi kukambirana

  • werengani ndime yonse pomwe Yesu amatuma ophunzira ake 72 pa Luka 10:1-24.Muonenso momwe Yesu amachitira ngati mtsogoleri ndi momwe ndimeyi ikuwonetsera machitidwe oti,Thamangirani ku Cholinga Chachikulu.
  • mu bundwe lomwe ine ndili,kodi cholinga chathu chachikulu  ndichotani?kodi chimaonetsera bwino komwe tikupita ?kodi limathandiza aliyense kudziwa tanthauzo ndi cholinga pa maudindo awo?kodi limaonetsera bwino cholinga chathu chachikulu ndi nthawi yomwe ndizagwire?
  • Kodi mwakawirikawiri ndimalumikizana ndi omwe ndikuwatsogolera za mmene ntchito yawo ikuthandizira ku cholinga chachikulu?
  • Kodi poyera ndimazindikira kufunika kwa iwo omwe udindo wawo utha kuwoneka ngati waung'ono  kapena osagwirizana ndi masomphenya anga?

Mu mutu otsatirawu,tiwona mmene Yesu anakwezera chotchinga mmene amatuma ophunzira ake.

Kufikira nthawi ina, Ine wanu wa paulendo,

Jon Byler

Tumizani kwa anzanu omwe akufuna kutsatila
chitsanzo cha Yesu potsogolera ngati otumikira.Angathe kulembetsa mwaulere komanso kuona magawo akale.mukafuna kupeza magawo akale , dinani apa.Magawo awa amatanthauziridwa mchichewa ndi abusa Grace Kacheto Saizi, gracekacheto@yahoo.com

Reflections for Serving Leaders is published by Center for Serving Leadership and Jon Byler. Copyright, 2022

Unsubscribe   |   Modify your subscription   |   View online