Gawo #342, December 11, 2024

Kusankha Kwa Utsogoleri Kwa Paulo: Akonzekeletseni

Paulo anasankha Timoteo kuti aziyendela limodzi pa ulendo komanso kuti azakhale mtsogoleri wamtsogolo. Koma akadali ku Lusitra Paulo anazindikira kuti panafunika zokonzelela Timoteo asanafike poyenda ndi gulu.

Machitidwe a Atumwi 16

3 Paulo anafuna kumutenga pa ulendo, kotero anachita mdulidwe chifukwa cha Ayuda amene amakhala mʼderalo pakuti onse amadziwa kuti abambo ake anali Mgriki.

Atsogoleri ambiri amakono salabadila za mdulidwe ngati mbali ya pulogalamu yokuza atsogoleri! Koma titha kuphunzira zambiri kuchokela kwa chitsanzo cha Paulo cha momwe atsogoleri muutumiki amaxhitila pokonekeletsa omwe asankhidwa kukhala mugulu lawo.

Atsogoleri muutumiki amakonzekeletsa ena poika poyela dipo.

Timoteo mwachidziwikile anamva kuwawa pathupi lake pomwe amadulidwa ndipo pa mulingo umodzi omwe unakwanilitsa cholinga cha Paulo. Koma pa mulingo ozamilapo, Paulo amaphunzitsa Timoteo kuti utsogoleri umakhudzana ndi kupweteka komanso nsembe. Paulo asanatenge sitepe yake yoyamba pa ulendo, ankafunika kuti naye apelekepo dipo ndipo Paulo ankafuna kuti awonetsetse kuti Timoteo waikamo "khungu nayenso". Ankafuna angoona zolinga za Timoteo. Kodi Timoteo ankangofuna chabe polowa ndi chochita pamoyo wake? Kapena anali okonzeka kupeleka dipo la utsogoleri? Nkuthekatu Paulo anali ataphunzilapo phunzilo lowawa kuchokela pa zomwe anakumana nazo ndi mtsogoleri wina wachichepele, Marko,yemwe anapita pa ulendo oyamba. Marko anabwelera pomwe zinthu zinafika povuta. (Onani Machitidwe 13:5,13;15:36-41) Mwanjila iliyonse, Paulo anaonetsetsa kuti Timoteo wamvetsetsa kuti utsogoleri ndi ulendo omwe umanyamula dipo.

Atsogoleri ena amayesetsa kulimbikitsa atsogoleri omwe akuphuka kumene kuti alowe muutsogoleri poika chindunji chawo pa phindu kapena ubwino okhala mtsogoleri ndipo amatsindika pa mphotho. Koma atsogoleri muutumiki amaika kuwawa kwake Kwa utsogoleri pa ndandanda ndipo amazindikira kuti ngati mtsogoleri watsopano sangadutse mulingo,sanakonzeke kukhala mtsogoleri. Akhoza kupeleka ntchito yovuta kuti awone ngati mtsogoleri watsopanoyu angadzuke ndikufikila kuvutolo ndi cholinga chabwino. Atsogoleri muutumiki amakonzekeletsa ena poika poyela dipo.

Atsogoleri muutumiki amakonzekeletsa ena pothana ndi chotchinga.

Ngati Paulo analola Timoteo,muyuda, kuti akhale osadulidwa, zikanakhala mlamdu waukulu kwa Ayuda onse. Pomwe Paulo ankakana kuti anthu amitundu Ina sankafunika mdulidwe, sadafune kuti kuthekela Kwa Timoteo kofikila ena kupondelezedwe. Choncho, anathana ndi chotchingacho chomwe chinali pa Timoteo ndipo chinali chovuta kwambili. Atsogoleri ena amasiya zotchinga kapena amayembekezela mtsogoleri wachichepele kuti aphunzile zonse paokha. Koma atsogoleri muutumiki amafunafuna njira zochosela zotchingazo. Pomwe ululu uli ofunika kuti zolinga zitsimikizike, atsogoleri muutumiki amasakasaka kuthana ndi zikhomo zilizonse zomwe zitha kulepheletsa kagwilidwe ka ntchito kabwino ka mtsogoleri yemwe ali watsopano.

Atsogoleri muutumiki amakonzekeletsa ena popeleka zofunika kuti achitebwino

Poona kufunika koti Timoteo adulidwe Paulo amamupatsa zida kuti achitebwino ngati mtsogoleri. Timoteo akadapanda kudulidwa sakadatha kumalowa mmasunagoge momwe Paulo nthawi zonse ankalowa poyamba akafuna kuti adzale mpingo. Komanso sakadatha kuzatsogolela bwino mpingo omwe unali ndi okhulupilira a chi Yuda. Choncho,ndi mdulidwe, Paulo anamukonzekeletsa Timoteo kuti apambane.

Atsogoleri ena amaika chidwi chawo pa chipambano cha iwo okha ndipo amaona gulu lawo ngati njira yothandizila. Koma atsogoleri muutumiki amaika chidwi pa zomwe gulu lawo limafuna ndipo amawapatsa zida zofunika kuti achitebwino. Atsogoleri muutumiki amaika mulingo wa kupambana kwawo poona kupambana Kwa ena.

Zoti tilingalire ndi kukambirana:

  • Ganizilani munthu amene mukumuona kuti ali ndi kuthekela wamugulu lanu, kapena membala watsopano yemwe mukumuganizila kuti akwele afike pa udindo wapamwamba. Kodi mutsata ndondomeko ziti kuti muwathandize kupeleka dipo pa kusintha komwe kumeneko?
  • Paulo amagwilitsa ntchito ululu poika poyela dipo la utsogoleri. Koma anachotsanso zotchinga pa Timoteo.Kodi mumapanga bwanji chiganizo pomwe pali kufunikila kuti ululu wina ufike ndi pomwe chotchinga chikufunika kuti chichosedwe kwa omwe mumawatumikila?
  • Pezani mtsogoleri mmodzi wachichepele mugulu lanu. Kodi chotchinga chomwe amakumana nacho ndichotani ndipo mungawachotsele bwanji?
  • Kodi ndimunjila ziti zomwe mukukonzekeletsa gulu lanu kuti lipambane? Kodi mungapange zotani poonjezela poonetsetsa kuti akhale opambana?

 

Mpaka nthawi Ina,

 

Ine wanu wapaulendo,

Jon Byler

Muphunziro lotsatirali, tiona momwe Paulo anaonetsela omwe anali mutsogoleri wake kuti angatsogolere motani.

Kuti mulandile izi pa WhatsApp dinani apa

 

Kuti muone maphunziro a m'buyomu, dinani apa.

Tumizani kwa anzanu omwe akufuna kutsatila chitsanzo cha Yesu potsogolera ngati otumikira. Angathe kulembetsa mwaulere komanso kuona magawo akale.mukafuna kupeza magawo akale, dinani apa. Magawo awa amatanthauziridwa mchichewa ndi abusa Grace Kacheto, gracekacheto@yahoo.com

Reflections for Serving Leaders is published by Center for Serving Leadership and Jon Byler. Copyright, 2024

Unsubscribe   |   Modify your subscription   |   View online