jpeg

Gawo #331, June 5, 2024

Barnaba: Kutumikira Munjila Yopembedza Ambuye.

Atsogoleri Muutumiki akhoza kuphunzira zochita zambiri kuchokela Kwa Barnaba zomwe zingawonjezele luso la utsogoleri wawo ndi kuthekela kwawo. Taonapo kale za Kutumikira kwake popeleka, polimbikitsa ndi kugwila ntchito kwake ngati gulu. Tikaonetsetsa nkhani yake ikuonetsela mmene chikhalidwe chake chiliri.

Machitidwe a Atumwi 13

1 Mu mpingo wa ku Antiokeya munali aneneri ndi aphunzitsi awa: Barnaba, Simeoni, Lukia wa ku Kurene, Manayeni (amene analeredwa pamodzi ndi mfumu Herode), ndiponso Saulo. 2 Iwo pamene ankapembedza Ambuye ndi kusala kudya, Mzimu Woyera anati, “Mundipatulire Barnaba ndi Saulo kuti akagwire ntchito imene ndinawayitanira.” 3 Ndipo atasala kudya ndi kupemphera anasanjika manja awo pa iwo nawatumiza.

Kodi Barnaba ndi gulu lake la atsogoleriwa amatani? Kodi amalingalira za mtsogolo? Kupanga ndondomeko ya zomwe azachite mu zaka zisanu zikubwela? kukhazikitsa ndandanda wa zinthu zoti achite kuti akwanilitse  masomphenya amtsogolo? Pomwe zochitika zonsezi zili zoyenera, gulu limeneli "limapembedza Mulungu ndiponso kusala kudya..." Chitsanzo cha Barnaba chikuwonetsela momwe kupembedza kumasinthila atsogoleri muutumiki.

Kupembedza kumatumikila pa kusintha kwa mtima

Gulu limeneli la atsogoleri linasonkhana mu kupembedza. Mchitidwe wawo opembedza unali mwakufuna kwawo kuti chindunji chawo chikhale Cha kwa Mulungu. Anaika chindunji cha mitima ndi malingaliro awo pa Mulungu. Anasala chakudya ngati mchitidwe ozikaniza okha zomwe matupi awo amalakalaka. Kulambira kwawo kunasuntha kakhalidwe ka mitima yawo kutali ndi Iwo.Kupembedza kunasuntha chindunji chawo kuchoka pa iwo eni kufikila pa Mulungu.

Atsogoleri ambiri amaika chindunji kapena chidwi chawo pa zochitika kunja kwa utsogoleri ndipo zambiri zimachitika popanda kusintha kwa mtima. Koma zochitikazi zitha kukhala zozitumikira wekha pokhapokha patakhala  kusintha kwa mtima. Kupembedza kumatulutsa kusintha kwa mtima. Kupembedza kunasuntha chidwi cha mtima kuchoka pa iwe, masomphenya athu, mapulani ndi maloto, ndikusitha mitima yathu kuloza kumwamba ndi kunja. Kusintha kwa mtimaku ndi kozungulira ndipo kumakonzekeletsa tsogoleri yemwe akutumikila kuti atumikire ena mosavuta. Zimapatsa kuthekela mtsogoleri kuti akhale ndi chindunji chake ku zakumwamba koposa pa chidwi cha iyemwini. Kupembedza kumawumba zolinga za mitima yathu ndipo kumapanga khalidwe. Mitima yathu ndiyofunika! khalidwe lathu ndiyofunika! Kusintha kwa mtima ndi kofunika kuti tikhale osadzikonda tokha zomwe utsogoleri otumikila umafuna. Utsogeri weniweni otumikila anthu umayamba ndi mtima osinthika pomwe wakumana ndi Mulungu.

Kupembedza kumatumikila posintha mutu

Munthawi yomwe gulu limeneli linkapembedza, anamva chitsogozo chomveka bwino cha Mzimu Oyera. Popanda kupembedza kapena kulambira, akanatha kuika chidwi cha malingaliro awo polimbikitsa mpingo omwe unalipo kale ku Antiokea. Koma popembedza amapezeka kuti asintha maganizo awo ndi chindunji chawo. Kulambira kumabweletsa kusintha kwa maganizo. Atsogoleri ambiri amayesetsa kusintha kuganiza kwawo kuti akhale mtsogoleri opambana. Koma atsogoleri muutumiki amazindikira kuti kupembedza kumasintha kuganiza kwawo mofunikira.

Kupembedza kumatumikila posinthana manja

Atamvetsela malangizo a Mzimu Oyera, gulu linaika manja pa Barnaba ndi Saulo ndikuwatumiza. Lingalirani kupambana kwa nchitidwewu. Awiriwa anali atsogoleri akulu akulu ampingo ndipo tsopano awachotsa nkuwatumiza kwinakwake! Izi zinali zadzidzidzi ndi zosayembekezeka. Kupembedza kumatulutsa kusintha kwa kachitidwe kazinthu. Atsogoleri muutumiki amalolera Mulungu awatsogolere mu njira zatsopano pomwe akupembedza. Mitima ndi mitu zomwe ndi zosinthika zotsatila zake ndi kusintha kwa zochitika zomwe zili mmanja . Machitidwe enieni a utsogoleri amatuluka mu kupembedza.

Zoti tilingalire ndi kukambirana

  • Kodi kulambira kwa Barnaba kukundiphunzitsa chani ine ngati mtsogoleri? Kodi msabatayi ndichite chani ngati mtsogoleri kuti ndikhale monga Iyeyu?
  • Kodi mtima wanga wasintha munjila ziti nditakumana ndi Mulungu? Kodi chizindikilo Cha ichi  ndichotani chomwe ndaona msabata yapitayi? Ngati palibe chizindikilo, kodi chikusowa muutsogoleri wanga ndichani ndipo ndikufunika ndisinthe pati?
  • Kodi ndapeza njila zoika nthawi yapadela ya kupembedza ndi kulambira mu kalendala yanga ya utsogoleri? Ngati ndi choncho, kodi pali njira yomwe nthawi zapadelazi zingalimbikitsike mwakusangalatsidwa kwanga? Ngati sichoncho, kodi nditsate ndondomeko ziti musabatayi kuti ndisinthe?
  • Ngati ndikutsogolera anthu omwe samaona kufunika Kwa kulambira pa mtsogoleri, kodi ndingachitepo chani kuti nditsogolere bwino popanda kupangitsa kupalamula mulandu osafunika?

Mpaka nthawi Ina, ine wanu wapaulendo,

Jon Byler

 

Muphunziro lotsatirali, tiona momwe Barnaba anatumikilira ndi kupeza kwake.

Kuti muone maphunziro a m'buyomu, dinani apa.

Tumizani kwa anzanu omwe akufuna kutsatila chitsanzo cha Yesu potsogolera ngati otumikira. Angathe kulembetsa mwaulere komanso kuona magawo akale.mukafuna kupeza magawo akale, dinani apa. Magawo awa amatanthauziridwa mchichewa ndi abusa Grace Kacheto, gracekacheto@yahoo.com

Reflections for Serving Leaders is published by Center for Serving Leadership and Jon Byler. Copyright, 2024